Pulezidenti Lazarus Chakwera watsimikizira mtundu wa a Malawi kuti nkhondo yolimbana ndi nthenda ya covid-19 ikutheka tsiku ndi tsiku ndipo kuti boma lake liyesetsa kuti muliliwu utheretu mdziko muno.
Polankhula mu uthenga wake ku mtundu wa Malawi kuchokera kunyumba ya boma ya Kamuzu mu mzinda wa Lilongwe Lamulungu lapitali pa Januwale 31, pulezidenti Chakwera mwa zina adati mwa anthu okwanira 17,334 omwe adayezedwa ngati ali ndi matenda a covid, anthu 5,027 okha ndamene adapezeka kuti ali ndi zizindikiro za matendawa, kuyimira anthu 29 mwa anthu 100 aliwonse omwe adayezedwa. Iye adati chiwerengerochi chatsika ndi anthu 8 pa 100 aliwonse poyaluzira msabata lapitalo pomwe anthu 37 mwa anthu 100 aliwonse adapezeka ndi kachirombo ka corona.
Pulezidenti chakwera adaonjezera kunena kuti polimbikitsa ntchito yomenyana ndi covid-19 boma lake lakhazikitsa malo oyezeramo matendawa okwanira 62 pomwe akuyembekezera kuti akwane 77, zipangizo zoyezera zokwana 51,500 zagawidwa kale dziko lonse ndipo kuti zina zokwana 150,000 zikusungidwa pomwe zinanso zikuyembekezeka kufika mdziko muno posachedwapa.
Mtsogoleri wadziko linoyu adapitilira mkulangiza mtundu wa a Malawi kuti nkhondoyi ikufunika kutsatira kwathunthu zitsogozo zomwe iye adakhazikitsa masabata apitawo ngati Malawi akufunitsitsa kupambana.
Pa za katemera wa matenda a covid pulezidenti Chakwera adatsimikizira a Malawi kuti akatswiri azdzayenera kuwunika mozama asadayambe kupereka katemerayo kuti adzaone ngati kuli koyenera kupereka kapena ayi, koma pulezidenti Chakwera adatsimikiza kuti boma lake chikuchita chilichonse chotheka kuti mulili wa Covid-19 usapitilire kufala komanso kutenga miyoyo ya mzika za dziko lino, ndipo adathokonza magulu onse omwe akuthandizira kuti ntchito yolimbana ndi matendewa ikhale ya phindu mdziko muno.
Mkulankhula kwawo a Chakwera sadanenepo kanthu ngati sukulu zomwe zinatsekedwa mongoyembekezera kamba kakufala kwa mulili wa covid zitsekulidweso posachedwapa kapena awonjezeraso nthawi ina pakutha pa masabata atatu omwe adalengeza kuti sukuluzi zikhale zotsekedwa.